Iwo Amene Amaiwala
()
About this ebook
Anthu opanduka samakumbukira zomwe zapangidwa kwa iwo ndipo nthawi zambiri amasankha kuiwala zinthu zina. Yudase sanakumbukire zimene Ambuye anamchitira, ndinso sanakumbukirenso zinthu zimene anaona ndi kumva kwa Yesu. Ichi ndi chifukwa chake adakhala mtundu wa munthu amene tikumudziwa lero ngati ‘Yudase’.
Kuthekera kokumbukira ndi chimodzi mwa zinthu zauzimu chomwe mtumiki atha kukhala nacho. Anthu amene samakumbukira, siwamba kuchita bwino. Iwo amalephera kufika mlingo wina. Bukhu lapaderali, pa mutu wosakambidwa kwambiriwu ndi mphamvu yochokera kwa Mulungu kwa inu.
Dag Heward-Mills
Bishop Dag Heward-Mills is a medical doctor by profession and the founder of the United Denominations Originating from the Lighthouse Group of Churches (UD-OLGC). The UD-OLGC comprises over three thousand churches pastored by seasoned ministers, groomed and trained in-house. Bishop Dag Heward-Mills oversees this charismatic group of denominations, which operates in over 90 different countries in Africa, Asia, Europe, the Caribbean, Australia, and North and South America. With a ministry spanning over thirty years, Dag Heward-Mills has authored several books with bestsellers including ‘The Art of Leadership’, ‘Loyalty and Disloyalty’, and ‘The Mega Church’. He is considered to be the largest publishing author in Africa, having had his books translated into over 52 languages with more than 40 million copies in print.
Read more from Dag Heward Mills
The Art of Leadership: 3rd Edition Rating: 5 out of 5 stars5/5Those Who Forget Rating: 5 out of 5 stars5/5Bible Memorisation Handbook Rating: 5 out of 5 stars5/5Ministerial Barrenness Rating: 5 out of 5 stars5/5Tell Them: 120 Reasons Why You Should Be a Soul Winner Rating: 4 out of 5 stars4/5The Mega Church: 2nd Edition Rating: 5 out of 5 stars5/5What it Means to be as Wise as a Serpent Rating: 5 out of 5 stars5/5Wisdom Is the Principal Thing for Your Ministry Rating: 0 out of 5 stars0 ratingsChurch Growth Rating: 5 out of 5 stars5/5The Art of Following Rating: 4 out of 5 stars4/5Model Marriage Rating: 4 out of 5 stars4/5Handbook Of Ceremonies Rating: 4 out of 5 stars4/5The Anointed and His Anointing Rating: 5 out of 5 stars5/51000 Micro Churches Rating: 0 out of 5 stars0 ratingsFruitfulness Rating: 5 out of 5 stars5/5Demons And How To Deal With Them Rating: 5 out of 5 stars5/5Anagkazo - Compelling Power! (2nd Edition) Rating: 5 out of 5 stars5/5
Related to Iwo Amene Amaiwala
Related ebooks
Day By Day With D.L. Moody Rating: 0 out of 5 stars0 ratingsGod Is Not Looking for a Part-Time Lover but a Committed People: It's Time to Stop Straddling the Fence Rating: 0 out of 5 stars0 ratingsHow Can I Say Thanks Rating: 0 out of 5 stars0 ratingsStop & Listen: God Is Talking to You Rating: 0 out of 5 stars0 ratingsAre You Holy? Rating: 0 out of 5 stars0 ratingsCorrection for the Church, Says God Rating: 0 out of 5 stars0 ratingsThe Honour of Representing God Rating: 0 out of 5 stars0 ratingsLiving or Dead?: A Series of Home Truths Rating: 5 out of 5 stars5/5To Belong: My Seed in the Ground Speaks Louder than Any Enemy's Voice Rating: 0 out of 5 stars0 ratingsMove from Failure to Success!: Discovering the Hidden Secrets of the Prayer of Hannah Rating: 0 out of 5 stars0 ratingsDaily Gems: The D. L. Moody Year Book: A Living Daily Message from the Words of D. L. Moody Rating: 0 out of 5 stars0 ratingsThe Struggles of a Christian Rating: 0 out of 5 stars0 ratingsGod Made Mankind, Why? Rating: 0 out of 5 stars0 ratingsRevelation: Removing the Prophetic Veil Bible Lesson 2 Rating: 0 out of 5 stars0 ratingsGolden Nuggets From God's Word Rating: 0 out of 5 stars0 ratingsDismantle Those Idols (Idolatry Exposed): 2nd Edition Rating: 4 out of 5 stars4/5Speak The Word Rating: 0 out of 5 stars0 ratingsReal Salvation Rating: 0 out of 5 stars0 ratingsLessons of the Prophets Part One Rating: 0 out of 5 stars0 ratingsThe Restoration Era Rating: 0 out of 5 stars0 ratingsI am Searching for my Lost Donkey!: My Weekly Milk, #16 Rating: 0 out of 5 stars0 ratingsIwo Amene Amakusiya Rating: 0 out of 5 stars0 ratingsGod Is Enough: Encouragement for Heavy Hearts Rating: 0 out of 5 stars0 ratingsSummary of Bishop of Hippo Saint Augustine's The Confessions (Oxford World's Classics) Rating: 0 out of 5 stars0 ratingsYourself Rating: 0 out of 5 stars0 ratingsZen from Len 3: The Journey Rating: 0 out of 5 stars0 ratingsAnti-Calvinism Rating: 0 out of 5 stars0 ratingsToo Soon to Quit! Rating: 0 out of 5 stars0 ratingsHow to Listen to God Rating: 5 out of 5 stars5/5How I Became God's Enemy Rating: 0 out of 5 stars0 ratings
Christianity For You
Anxious for Nothing: Finding Calm in a Chaotic World Rating: 4 out of 5 stars4/5Boundaries Updated and Expanded Edition: When to Say Yes, How to Say No To Take Control of Your Life Rating: 4 out of 5 stars4/5The Screwtape Letters Rating: 4 out of 5 stars4/5Mere Christianity Rating: 4 out of 5 stars4/5Decluttering at the Speed of Life: Winning Your Never-Ending Battle with Stuff Rating: 4 out of 5 stars4/5The Good Girl's Guide to Great Sex: Creating a Marriage That's Both Holy and Hot Rating: 4 out of 5 stars4/5Present Over Perfect: Leaving Behind Frantic for a Simpler, More Soulful Way of Living Rating: 4 out of 5 stars4/5The Four Loves Rating: 4 out of 5 stars4/5The Purpose Driven Life: What on Earth Am I Here For? Rating: 4 out of 5 stars4/5Good Boundaries and Goodbyes: Loving Others Without Losing the Best of Who You Are Rating: 5 out of 5 stars5/5The Bible Recap: A One-Year Guide to Reading and Understanding the Entire Bible Rating: 5 out of 5 stars5/5Law of Connection: Lesson 10 from The 21 Irrefutable Laws of Leadership Rating: 4 out of 5 stars4/5The 5 Love Languages: The Secret to Love that Lasts Rating: 4 out of 5 stars4/5Boundaries Workbook: When to Say Yes, How to Say No to Take Control of Your Life Rating: 4 out of 5 stars4/5The 21 Irrefutable Laws of Leadership: Follow Them and People Will Follow You Rating: 4 out of 5 stars4/5Uninvited: Living Loved When You Feel Less Than, Left Out, and Lonely Rating: 4 out of 5 stars4/5Boundaries with Kids: How Healthy Choices Grow Healthy Children Rating: 4 out of 5 stars4/5The Stories We Tell: Every Piece of Your Story Matters Rating: 3 out of 5 stars3/5Changes That Heal: Four Practical Steps to a Happier, Healthier You Rating: 4 out of 5 stars4/5Girl, Wash Your Face: Stop Believing the Lies About Who You Are so You Can Become Who You Were Meant to Be Rating: 3 out of 5 stars3/5Wild at Heart Expanded Edition: Discovering the Secret of a Man's Soul Rating: 4 out of 5 stars4/5Less Fret, More Faith: An 11-Week Action Plan to Overcome Anxiety Rating: 4 out of 5 stars4/5Everybody, Always: Becoming Love in a World Full of Setbacks and Difficult People Rating: 4 out of 5 stars4/5NIV, Holy Bible Rating: 4 out of 5 stars4/5Winning the War in Your Mind: Change Your Thinking, Change Your Life Rating: 5 out of 5 stars5/5Warrior of the Light: A Manual Rating: 4 out of 5 stars4/5The Book of Enoch Rating: 4 out of 5 stars4/5Undistracted: Capture Your Purpose. Rediscover Your Joy. Rating: 5 out of 5 stars5/5
Reviews for Iwo Amene Amaiwala
0 ratings0 reviews
Book preview
Iwo Amene Amaiwala - Dag Heward-Mills
Kukhulupirika ndi Kusakhulupirika
Iwo Amene
AMAIWALA
DAG HEWARD-MILLS
Kupatula ngati kutchulidwa kwina, Malemba onse achokera mu Baibulo la Bukhu Lopatulika La Chichewa 1966
Umwini © 2019 Dag Heward-Mills
Mutu Woyambirira: Those who Forget
Kutsindikiza koyamba 2019 ndi Parchment House
Dziwani zambiri zokhudza Dag Heward-Mills pa:
Healing Jesus Campaign
Lemberani kwa: evangelist@daghewardmills.org
Webusaiti: www.daghewardmills.org
Facebook: Dag Heward-Mills
Twitter: @EvangelistDag
ISBN:
Umwini wonse wasungidwa pansi pa umwini lamulo la umwini lapadziko. chilolezo cholembedwa chikuyenera kutengedwa kuchokera kwa wosindikiza kuti mugwiritse ntchito kapena kutulutsa kachikena gawo lili lonse la bukhu limeli, pokha pokha mawu ochepa mu maganizo ofunikira kwambiri kapena nkhani
Zamkatimu
Kusalungama kwa Iwo Amene Amaiwala 1
Zifukwa Zisanu ndi Chimodzi Za kufunika kwa Kukumbukira 13
Zoipa zisanu Zimene Zimagwera Anthu Amene Amayiwala 22
Zolakwika Zisanu ndi Zitatu Zomwe Anthu Amakonda Kuiwala 37
Mifungulo Isanu ndi Iwiri Yomwe Ikakuthandizeni Kukumbukira 60
Zinthu Zomwe Anthu Olungama Amakumbukira 73
Zotsatira Zisanu ndi Ziwiri za Kukumbukira 83
Anthu Omwe Simukuyenera Kuwaiwala 87
Zikumbutso Zisanu Zomwe Zimalimbana ndi Kuiwala 96
Mutu 1
Kusalungama kwa Iwo Amene Amaiwala
... Mulungu sali wosalungama kuti adzaiwala...
Ahebri 6:10
1. ANTHU AMENE ALI OIWALA NDI OSALUNGAMA.
PAKUTI MULUNGU SALI WOSALUNGAMA KUTI ADZAIWALA nchito yanu, ndi cikondico mudacionetsera ku dzina lace, umo mudatumikira oyera mtima ndi ku-watumikirabe.
Ahebri 6:10
Anthu ambiri amadziwa za machimo aakulu anayi: kunama, kuba, dama ndi kupha. Ngati mu-tati mufunse anthu mndandanda wa machimo iwo sangathe kunena za tchimo la kuiwala. Koma Mawu a Mulungu ali omveka pa nkhaniyi. Kuiwala ndi kusalungama! Kuiwala, kulephera kuvo-mereza, kulephera kukumbukira ndi machimo pamaso pa Mulungu.
Kodi angathe namwali kuiwala zokometsera zace, kapena mkwatibwi zobvala zace? koma anthu anga andiiwala Ine masiku osawerengeka.
Yeremiya 2:32
Ndizosamvetsetseka kuganizira za zina zomwe anthu osalungama amaiwala.
Lemba lopatulika pa nkhani ya kubwerera mmbuyo limasonyeza momwe mkwatibwi sadzaiwala diresi lake laukwati. Diresi laukwati ndi chinthu chofunikira kwambiri kwa mkwatibwi.
Akwatibwi ambiri amalongosola za diresi lawo laukwati mwansanga, nthawi yaukwati isanafike. Mu Lemba ili, kupusa koiwala Mulungu kukufaniziridwa ndi kuthekera kosayerekezeka kuti mkwatibwi adzaiwala diresi lake laukwati.
Anthu amakula ndikuiwala omwe anawasamalira, omwe anawadyetsa komanso omwe amawa-konda. Amayiwala omwe adawabweretsa kwa Khristu, omwe adawaukitsa mwa Ambuye ndi omwe anawaika mu utumiki. Kodi n’zotheka kuti anthu akhoza kuiwala anthu omwe adawathandi-za pa njira yofunikira kwambiri pamoyo wawo? Kodi angatembenuke ndikuukira anthu omwe an-awalera? Yankho ndi Inde
! Izi zimachitika nthawi zonse.
Anthu amaiwala Mulungu pamene apambana. Maiko a ku Ulaya asiya Mulungu chifukwa akhala opambana kwambiri. Koma ndi Mulungu amene anawapatsa zomwe ali nazo. Anthu amakhulupiri-ra kuti kulibe Mulungu akakhala mamiliyoneya. Ndi tchimo lokhumudwitsa kwambiri kuiwala amene anakupatsani zonse! Ndithudi, ndiko kusalungama kumene kuli koyenera chilango choopsa kwambiri.
2. ANTHU AMENE ALI OIWALA NDIWOSALUNGAMA NDIPO ALIBE CHIKHA-LIDWE CHA MULUNGU.
PAKUTI MULUNGU SALI WOSALUNGAMA KUTI ADZAIWALA nchito yanu, ndi cikondico mudacionetsera ku dzina lace, umo mudatumikira oyera mtima ndi ku-watumikirabe.
Ahebri 6:10
Mulungu samayiwala! Munthu amayiwala koma Mulungu samayiwala! Anthu oiwala alibe chikhalidwe cha Mulungu! Ndi chiwonetsero cha chikhalidwe chakugwa cha anthu oipa ndi anthu osokonezeka kuti aiwale zinthu zomwe siziyenera kuiwalidwa.
Munthu amene amalamulidwa ndi Mau a Mulungu ndi Mzimu wa Mulungu samayiwala zinthu zina.
Munthu wachilengedwe sakonda kukumbukira omwe adamuthandiza. Munthu wachilengedwe wosapulumutsidwa sakonda kukumbukira kumene adachokerako. Munthu wachilengwedwe safu-na kuti aliyense adziwe momwe adakhalira.
Koma ichi sichikhalidwe cha Mulungu. Pamene Yesu adayenda padziko lapansi adatiuza kumene adachokera. Iye anati Iye sakanakhoza kuchita kanthu mwa Iye yekha.
Iye anati Iye amangoyankhula mawu omwe Atate Ake anamupatsa Iye.
Izi zikusiyana kwambiri ndi munthu wonyada wa wauchimo. Munthu wonyada ndi woipa sa-mawulula chiyambi chake. Iye amakhulupirira kuti ali wodzipangira yekha ndipo amaganiza kuti iye anabwera powonekera ndi mphamvu yake.
3. ANTHU AMENE ALI OIWALA NDIWOSALUNGAMA NDIPO ADATEM-BEREREDWA KUTI AZAUMA.
Ngati gumbwa aphuka popanda cinyontho? Ngati mancedza amera popanda madzi? Akali auwisi, sanawaceka, AUMA, asanaume mathengo onse ena. Momwemo mayendedwe a ONSE OIWALA MULUNGU...
Yobu 8:11-13
Anthu oiwala anatembereredwa kuti azauma. Loyipa kwambiri ndi tchimo lakuiwala kuti matem-berero amagwera mmiyoyo ya anthu oiwala. Simukufunika kumva themberero likuneneredwa pa moyo wanu poiwala zinthu zofunikira. Malemba Opatulika adalengeza kale kuti iwo akuiwala Mulungu adzafota. Samalani kuti mukumbukire njira zonse zomwe Ambuye akubweretsani inu ndi zinthu zonse zomwe Iye wakuchitirani.
4. ANTHU OSALUNGAMA SAMAKHALA TCHELU NDI ZOYIPA ZOMWE ZIMAZA CHIFUKWA CHAKUYIWALA
Ku mitsinje ya ku Babulo, Kumeneko tinakhala pansi, inde tinalira, Pokumbukila Ziyoni.
Pa msondodzi uli m’mwemo Tinapacika mazeze athu.
Popeza pamenepo akutigwirawo anatifunsa nyimbo, Ndipo akutizunza anafuna tisekere, Ndi kuti, Mutiyimbire nyimbo imodzi ya ku Ziyoni. Tidati, Tidzayimba bwanji nyimbo ya Yehova M’dziko lacilendo?
NDIKAKUIWALANI, YERUSALEMU, DZANJA LAMANJA LANGA LIIWALE LUSO LACE.
LILIME LANGA LIMAMATIKE KU NSAYA ZANGA, NDIKAPANDA KUKUM-BUKILA INU; Ndikapanda kusankha Yerusalemu Koposa cimwemwe canga copambana.
Masalmo 137: 1-6
Muyenera kuyamba kukumbukira kwambiri. Amene analemba bukhu la Masalmo anadziwa kuti zingakhale zovuta kuiwala Yerusalemu. Anadzitemberera yekha ngati sakumbukira kumene anachokera. Umu ndi momwe nkhani ya chikumbutso ilili ya patali. Mwinanso mukhoza kungosi-ya kukhala ndi moyo ngati simukukumbukira zinthu zina zake. Lilime lanu lidzagwirana ndi denga la pakamwa panu ngati simungathe kukumbukira komwe Mulungu anakuukitsani. Dzanja lanu lamanja silingathe kulemba cheke pamene mukuiwala zomwe Mulungu wakuchitirani.
5. ANTHU OSALUNGAMA AMAYIWALA AKAKHUTA, AKAKHALA NDI NYUMBA NDIPONSO AKALEMERA.
KUTI, MUTADYA NDI KUKHUTA, NDI KUMANGA NYUMBA ZOKOMA, ndi ku-khalamo; ndipo zitacuruka ng’ombe zanu, ndi nkhosa zanu, zitacurukanso siliva wanu ndi golidi wanu, zitacurukanso zonse muli nazo; mtima wanu ungatukumuke, nimungaiwale Yehova Mulungu wanu, amene anakuturutsani m’dziko la Aigupto, m’nyumba ya akapolo;
Deuteronomo 8: 12-14
Kusalungama kwa kuyiwala kawirikawiri kumakhudza anthu omwe ali odzaza! Anthu omwe amakhala m’nyumba zawo amakonda kumayiwala Mulungu. Iwo omwe awonjezera zonse zomwe ali nazo amaiwalanso Mulungu mwansanga. Muyenera kukhala mtundu wa munthu yemwe ali wolemera ndi wochita bwino koma wokumbukira kumene mudachokera. Ndizomvetsa chisoni kuti ambiri olemera amalankhula zambiri koma amapereka pang’ono. Anthu amalankhula za madalitso omwe Mulungu wa wapatsa koma samalemekeza Mulungu chifukwa cha zomwe wachita.
6. ANTHU OSALUNGAMA AMENE AMAYIWALA NTHAWI ZAMBIRI AMAKHA-LA ANTHU ODZIKWEZA.
Kuti, mutadya ndi kukhuta, ndi kumanga nyumba zokoma, ndi kukhalamo; ndipo zitacuruka ng’ombe zanu, ndi nkhosa zanu, zitacurukanso siliva wanu ndi golidi wanu, zitacurukanso zonse muli nazo; MTIMA WANU UNGATUKUMUKE, nimungaiwale Yehova Mulungu wanu, amene anakuturutsani m’dziko la Aigupto, m’nyumba ya akapolo; ndipo munganene