Iwo Amene Amakusiya
()
About this ebook
Anthu amene amakusiya atha kukuwonongani. Palibe chimene chingalongosera kumva kwa kukhumudwa, kubalalika ndi nkhawa zimene zimadza pamene anthu akukusiyani. Bukhu ili lalembedwa kukuthandizani inu kulimbana ndi chiwonongeko chomwe chimadza pamene anthu akusiyani. Musanyengedwe. Kusiidwa sikwachilendo kwa inu ndi utumiki wanu. Ambiri ena avutika ndi zomwezo. Satana anali wopanduka woyamba ndipo akulimbikitsa opandukira onse kuyambira pamenepo.
Ndi bukhu limeneri mu manja anu, muzachirimika ndi kulimbana ndi mzimu wa kusakhulupirika umene umadza ndi “iwo amene amakusiyani”.
Dag Heward-Mills
Bishop Dag Heward-Mills is a medical doctor by profession and the founder of the United Denominations Originating from the Lighthouse Group of Churches (UD-OLGC). The UD-OLGC comprises over three thousand churches pastored by seasoned ministers, groomed and trained in-house. Bishop Dag Heward-Mills oversees this charismatic group of denominations, which operates in over 90 different countries in Africa, Asia, Europe, the Caribbean, Australia, and North and South America. With a ministry spanning over thirty years, Dag Heward-Mills has authored several books with bestsellers including ‘The Art of Leadership’, ‘Loyalty and Disloyalty’, and ‘The Mega Church’. He is considered to be the largest publishing author in Africa, having had his books translated into over 52 languages with more than 40 million copies in print.
Read more from Dag Heward Mills
The Art of Leadership: 3rd Edition Rating: 5 out of 5 stars5/5Those Who Forget Rating: 5 out of 5 stars5/5Bible Memorisation Handbook Rating: 5 out of 5 stars5/5Ministerial Barrenness Rating: 5 out of 5 stars5/5Tell Them: 120 Reasons Why You Should Be a Soul Winner Rating: 4 out of 5 stars4/5The Mega Church: 2nd Edition Rating: 5 out of 5 stars5/5What it Means to be as Wise as a Serpent Rating: 5 out of 5 stars5/5Wisdom Is the Principal Thing for Your Ministry Rating: 0 out of 5 stars0 ratingsChurch Growth Rating: 5 out of 5 stars5/5The Art of Following Rating: 4 out of 5 stars4/5Model Marriage Rating: 4 out of 5 stars4/5Handbook Of Ceremonies Rating: 4 out of 5 stars4/5The Anointed and His Anointing Rating: 5 out of 5 stars5/51000 Micro Churches Rating: 0 out of 5 stars0 ratingsFruitfulness Rating: 5 out of 5 stars5/5Demons And How To Deal With Them Rating: 5 out of 5 stars5/5Anagkazo - Compelling Power! (2nd Edition) Rating: 5 out of 5 stars5/5
Related to Iwo Amene Amakusiya
Related ebooks
Those Who Leave You Rating: 5 out of 5 stars5/5Get Real: No Time for Games Rating: 0 out of 5 stars0 ratingsTurning Water into Wine: 100 Stories of God's Hand in Life Rating: 0 out of 5 stars0 ratingsIwo Amene Ali A Umbali Rating: 0 out of 5 stars0 ratingsIwo Amene Amaiwala Rating: 0 out of 5 stars0 ratingsHeart Condition: From Religiosity to Relationship with the Creator Rating: 0 out of 5 stars0 ratingsDismantle Those Idols (Idolatry Exposed): 2nd Edition Rating: 4 out of 5 stars4/5Satan's Sleeping Pills: Revivalist Series, #4 Rating: 0 out of 5 stars0 ratingsThe Lovable Antichrist Rating: 0 out of 5 stars0 ratingsHealing Your Church Hurt: What To Do When You Still Love God But Have Been Wounded by His People Rating: 4 out of 5 stars4/5DON'T DROP YOUR SALVATION: Lay Hold on Eternal Life 1 Timothy 6: 19 Rating: 0 out of 5 stars0 ratingsPastor, Don’T Let Satan Hijack Your Church Rating: 0 out of 5 stars0 ratingsThe Forgiving Soul: How to Forgive Yourself, Others and Life Rating: 0 out of 5 stars0 ratingsPray & Go: Your Invitation to Become a Great Commission Christian Rating: 0 out of 5 stars0 ratingsChurch Folk Going to Hell in a Hand Basket: Beguiled - From the Pulpit Through the Pews to the Exit Rating: 0 out of 5 stars0 ratingsThe Burning Heart: Restoring Your Spiritual Passion after Broken Dreams and Disappointments Rating: 0 out of 5 stars0 ratingsRadiance Following a Catastrophe Rating: 0 out of 5 stars0 ratingsAmbiri Aitanidwa Rating: 0 out of 5 stars0 ratingsSermons from a Potato Field Rating: 0 out of 5 stars0 ratingsYou Can Defeat Demons: A Practical Guide to Casting out Evil Spirits Rating: 3 out of 5 stars3/5Too Soon to Quit! Rating: 0 out of 5 stars0 ratingsالشَجرة وقِسّيْسِيَّتك Rating: 0 out of 5 stars0 ratingsBe On The Alert!! LionProwling Rating: 0 out of 5 stars0 ratingsOld Testament Stories for New Testament Strength Rating: 0 out of 5 stars0 ratingsWhy Churches Die: Diagnosing Lethal Poisons in the Body of Christ Rating: 3 out of 5 stars3/5The Most Offensive Book Ever Written Rating: 0 out of 5 stars0 ratingsSummary of Leonard Ravenhill's Why Revival Tarries Rating: 0 out of 5 stars0 ratingsOpen Your Eyes Rating: 0 out of 5 stars0 ratingsWhy Good People Mess Up: Keys to upright living in a seductive world Rating: 0 out of 5 stars0 ratings
Christianity For You
Winning the War in Your Mind: Change Your Thinking, Change Your Life Rating: 5 out of 5 stars5/5The 5 Love Languages: The Secret to Love that Lasts Rating: 4 out of 5 stars4/5The Purpose Driven Life: What on Earth Am I Here For? Rating: 4 out of 5 stars4/5The Bible Recap: A One-Year Guide to Reading and Understanding the Entire Bible Rating: 5 out of 5 stars5/5The Good Girl's Guide to Great Sex: Creating a Marriage That's Both Holy and Hot Rating: 4 out of 5 stars4/5The Book of Enoch Rating: 4 out of 5 stars4/5Your Brain's Not Broken: Strategies for Navigating Your Emotions and Life with ADHD Rating: 5 out of 5 stars5/5The Screwtape Letters Rating: 4 out of 5 stars4/5The Holy Bible (World English Bible, Easy Navigation) Rating: 4 out of 5 stars4/5Don't Give the Enemy a Seat at Your Table: It's Time to Win the Battle of Your Mind... Rating: 5 out of 5 stars5/5Mere Christianity Rating: 4 out of 5 stars4/5How to Lead When You're Not in Charge: Leveraging Influence When You Lack Authority Rating: 4 out of 5 stars4/5The 21 Irrefutable Laws of Leadership: Follow Them and People Will Follow You Rating: 4 out of 5 stars4/5Law of Connection: Lesson 10 from The 21 Irrefutable Laws of Leadership Rating: 4 out of 5 stars4/5Boundaries Updated and Expanded Edition: When to Say Yes, How to Say No To Take Control of Your Life Rating: 4 out of 5 stars4/5Warrior of the Light: A Manual Rating: 4 out of 5 stars4/5The Story: The Bible as One Continuing Story of God and His People Rating: 4 out of 5 stars4/5Girl, Wash Your Face: Stop Believing the Lies About Who You Are so You Can Become Who You Were Meant to Be Rating: 3 out of 5 stars3/5I'll Start Again Monday: Break the Cycle of Unhealthy Eating Habits with Lasting Spiritual Satisfaction Rating: 4 out of 5 stars4/5The Four Loves Rating: 4 out of 5 stars4/5Boundaries Workbook: When to Say Yes, How to Say No to Take Control of Your Life Rating: 4 out of 5 stars4/5The Unseen Realm: Recovering the Supernatural Worldview of the Bible Rating: 5 out of 5 stars5/5Uninvited: Living Loved When You Feel Less Than, Left Out, and Lonely Rating: 4 out of 5 stars4/5Changes That Heal: Four Practical Steps to a Happier, Healthier You Rating: 4 out of 5 stars4/5Less Fret, More Faith: An 11-Week Action Plan to Overcome Anxiety Rating: 4 out of 5 stars4/5Boundaries with Kids: How Healthy Choices Grow Healthy Children Rating: 4 out of 5 stars4/5Anxious for Nothing: Finding Calm in a Chaotic World Rating: 4 out of 5 stars4/5
Reviews for Iwo Amene Amakusiya
0 ratings0 reviews
Book preview
Iwo Amene Amakusiya - Dag Heward-Mills
Kukhulupirika ndi Kusakhulupirika
Iwo Amene
AMAKUSIYA
DAG HEWARD-MILLS
Parchment House
Kupatula ngati kutchulidwa kwina, Malemba onse achokera mu Baibulo la Bukhu Lopatulika La Chichewa 1966
Mutu Woyambirira: Those who Leave You
Copyright © 2019 Dag Heward-Mills
Kutsindikiza koyamba 2019 ndi Parchment House
Dziwani zambiri za Dag Heward Mills pa:
Healing Jesus Campaign
Email: evangelist@daghewardmills.org
Website: www.daghewardmills.org
Facebook: Dag Heward-Mills
Twitter: @EvangelistDag
ISBN : 978-1-64135-863-7
Umwini wonse wasungidwa pansi pa lamulo lachitsindiziko lachilungamo. Chilolezo cholembera chiyenera kutetezedwa kuchokera kwa wofalitsa kuti agwiritse ntchito kapena kubwerezanso gawo lirilonse la bukhu ili, kupatulapo ndemanga zochepa mu ndemanga zakuya kapena nkhani.
Zamkatimu
Mutu 1: Chifukwa Chomwe Mulungu Amalolera Anthu Kukusiyani
Mutu 2: Ziwanda Zomwe Zimagwira Mwa Anthu Amene Amachoka Mwaupandu
Mutu 3: Mawu Osayankhulidwa a Iwo Amene Amakusiyani
Mutu 4: Zoneneza za Iwo Amene Amakusiyani
Mutu 5: Momwe Iwo Amene Amakusiyani Amakhalira Chitsanzo Choipa
Mutu 6: Momwe Mbewu za Kusakhazikika Zimafesedwera Ndi Iwo Amene Amakusiyani
Mutu 7: Mbewu za Kukhazikika
Mutu 8: Masoka a Iwo Amene Amakusiyani
Mutu 9: Momwe Mungadziwire Iwo Amene Atadzakusiyeni
Mutu 10: Momwe Mungamenyanirane ndi Mimbulu
Mutu 11: Zotsatira Zomwe Amene Amachoka ndi Ana Athu Ayenera Kuyembekezera
Mutu 12: Mmene Mungapempherere Amene Amapangitsa Mavuto Pamene Akusiyani
Mutu 1
Chifukwa Chomwe Mulungu Amalolera Anthu Kukusiyani
Zifukwa Khumi Ndi Zisanu Zomwe Mulungu Amalolera Anthu Kukusiyani
Pali zifukwa zambiri zomwe Mulungu amalolera kuti anthu akusiyeni ngakhale kukupweteketsani mtima.
1. Yehova amatha kulola anthu kuti akusiyeni pofuna kukozanso zolakwika pamaziko a utumiki wanu.
Poyamba utumiki uli wonse, timadzadzidwa ndi mantha makamaka a kulephera. Mantha a kulephera amapangisa ife kutenga thandizo lililose lomwe lapezeka. Poyesetsa kupeza chithandizo, atumiki ambiri amakhala mbali ya anthu olakwika.
Abrahamu ndi chitsanzo chabwino pa izi. Mulungu anamuuza kuti azisiyanitse ku banja lake ndikuenda ulendo wawutali komanso wachinsinsi kupita ku dziko lachilendo lolonjezedwa. Mmalo modzisiyanitsa ku banja lake monga Mulungu ananenera, Abrahamu anapita ndi azibale ake ena mmodzi mwa iwo odziwika anali Loti.
Ndipo Yehova anati kwa Abramu, tuluka iwe dziko lako, ndi KWA ABALE AKO, ndi ku nyumba ya atate wako kunka kudziko limene ndizasonyeza iwe.
Genezesi 12:1
Ndipo ankwera abramu kuchoka ku Aigupto, iye ndi mkazi wake, ndi zose anali nazo, ndi LOTI PAMODZI NAYE kunka ku dziko la kumwera.
Genezesi 13:1
Mavuto onse omwe Abrahamu anakumana nawo anachokera pa kupezeka kwa Loti pa moyo wake. Onani mavuto omwe Abrahamu anakumana nawo chifukwa cha Loti.
1. Abrahamu anali ndi mavuto a mikangano ndi chisokonezo chifukwa cha Loti. Abrahamu m’kupita kwa nthawi anazisiyanitsa kwa abale ake chifukwa cha Loti (Genezesi 13:7-8).
2. Abrahamu anamenya nkhondo yomwe sankayenera kumenya chifukwa cha Loti. Abrahamu analanditsa Loti mmanja mwa mfumu Kedorelaomere (Genezesi 14:1-16)
3. Abrahamu anapembedzera maka chifukwa cha Loti. Abrahamu anayenera kupulumusa mphwake kuchionongeko cha Sodomu ndi Gomora (Genezesi 18:23-33)
Izi ndi zomwe ndimazitcha zolakwika pa maziko a utumiki. Ndi cholakwika chomwe munthu umapanga poyamba utumiki, ndipo zimadza kamba ka mantha. Zolakwazi zimapangisa anthu olakwika kukhala kumbali yako ngati goli (chipsinjo) pa zonse zomwe umapanga.
Nthawi zina anthu amakwatira anthu olakwika akamalowa mu utumiki.Mulungu amatha kuchotsa anthu olakwika omwe mwakwatirana nawo pa dziko lapansi pofuna kukumasulani ku goli (chipsinjo) mu m’khosi mwanu.
Anthu ena omwe anali mbali ya utumiki wanga poyamba salinso mbali ya zomwe ndimapanga pano. Mwina, Ndinawatenga ena mwa iwo chifukwa ndimaopa kuti sindikwanitsa popanda iwo. Kupezeka kwawo kumandipatsa chilimbikitso choti ndipambana. Mulungu mwa zifundo zake anapangitsa kuti ena mwa iwo andisiye. Ngakhale ena mwa iwo ndimawasowa, ndinazindikira kuti Mulungu anawalola kundisiya chifukwa chinali cholakwitsa poyamba kuwatenga mu maso mphenya omanga mpingo.
2. Yehova amatha kulola anthu kuti akusiyeni pofuna kuti mudzichepetse
Ndipo mukumbukile njira yonse imene Yehova Mulungu wanu anakuyendesani m’chipululu zaka izi makumi anai, KUTI AKUCHEPETSENI, kukuyesani kudziwa chokhala mumtima mwanu, ngati mudzasunga malamulo ake, kapena iai.
Deuteronomo 8:2
Ndi zokumana nazo zakudzichepesa kusiidwa, kutaidwa kapena anthu kusiya kugwira nawe ntchito limodzi. Kuchoka kuli konse kumasiya kuwawasa mkamwa mwanu. Nthawi zose munthu akachoka mwadzidzidzi, amasiya mmbuyo manfuso opanda mayankho. Zosayembekezereka zomwe zimalengedwa ndi anthu zimasiya mavuto ndi kudzichepesa kwenikweni.
Kutatha kubzala ma tchalitchi kwa zaka zambiri, ndinadalitsidwa pokhala ndi mazana a azibusa, anyamata ndi atsikana okhulupirika. Ndinadalitsikaso kukhala ndi ena mwa abale anga kukhala azibusa mu mpingo.
Komabe, tsiku lina ena mwa achibale anga anandisiya mu utumiki ndikuyamba kupanga zosemphana ndi zomwe ndimaphunzitsa. Chinali chamanyazi kwa ine momwe achibale anga amalimbana ndi kupandukira komanso kusakhulupirika mu mpingo. Tsopano ndinaenera kumenyana ndi banja langa lomwe. Izi zakhala zikundibwerera kangapo kuti ndakhala ndikukwanitsa kupanga anthu ena ambiri kukhala okhulupirika koma kulephera kutero ku banja langa lomwe.
Ndipo ndinazindikila kuti Mulungu amafuna ndizichepetse mu njira imeneyi. Iye anafuna kundionesa kuti sikuthekera kapena mphamvu kapena chiphunzitso kapenanso ulamuliro koma chisomo chake chokha. Mwina, muli ndi anthu ena omwe anakusiyani. Lolani Mulungu agwire ntchito yake muuzimu yokuchepetsani ku ntchito yake.
3. Ambuye amatha kulola anthu akusiyeni chifukwa mwalola kuti mamembala anu akhale osadziwa posawaphunzitsa za kukhulupirika ndi kusakhulupirika
Ndipo pamodzi ndi Abisalomu panapita anthu mazana awiri aku Yerusalemu ndiwo oitanidwa, namuka m’kupulukira kwawo, osadziwa kanthu.
2 Samueli 15:11
Satana anadya mwa anthu omwe samadziwa (mbuli). Chinyengo nthawi zose chimachulukira pamene anthu sanaonesedwe poyera chilungamo cha mawu. Absalomu anali yekhayo yemwe anakwanisa kutsogolera azimbambo mazana awiri omwe anali ofooka (ophweka) mmalingalilo. Kufooka mmalingalilo kumeneku timakutchaso kusadziwa (umbuli).
Mfundo za kukhulupirika ndi kusakhulupirika, utate ndi chikumbukiro sizimakonda kuphuzitsidwa mu mipingo. Ndizosadabwitsa mamembala a mumpingo amakhala nyama zophweka za ziwanda za chinyengo zomwe zimadya pa kusadziwa kwawo. Mwina, mwalola kusadziwa pa maphunziro awa kuyende ndi kufala kwa mpingo. Satana watengerapo mwayi pa kusadziwa ndi kuchititsa chisokonezo pakati panu.
Eya, mpingo wanu utha kuthala odalitsidwa ndi ma uthenga a kuchitabwino, ukwati ndi machilitso koma palibe mwa maphuzitso awa angateteze mpingo wanu ku ziwanda za kusakhulupirika ndi chinyengo.
Tsiku lina, mbusa wina anandifusa chifukwa chani ndimaphunzitsa za kukhulupirika ndi kusakhulupirika. Moselewula anaonjezera kuti, khululupirika si chinthu choti mkuphuzitsa. Ndichomwe umangolamula.
Ndipo anapitiliza nati, Ndimakhalidwe anu abwino, umalamula khulupirika kwa anthu amene akuzungulira.
Posachedwa patatha izi anakanthidwa ndi chinyengo chowawa kuchokera kwa abwenzi ake omwe. Sanakhulupirire kuti izi zimachitika kwa iye. Atakumana ndi izi, kunyogodola pa mabuku ndi ziphuzitso zanga zinasandulika kukhala zozizwitsa. Iye anakhala mmodzi mwa osirira pa maphuziro a kukhulupirika ndipo anayamba kulimbikitsa mabuku anga yekha. Mkutheka simungaziwe ubwino wa kuphunzitsa pokhapokha mutakumana ndi zotsatira za kusadziwa.
4. Yehova amatha kulola anthu ena akusiyeni chifukwa munanyoza mtumiki mzanu pamene mpingo wake unagawanikana
…wokondwera ndi tsoka sadzapulumuka chilango
Miyambi 17:5
Nthawi zambiri, timanyoza anthu akakhala mmavuto. Ngat anzake a Yobu timaoneka odziwa zifukwa zomwe zinthu zoipa zikuchitika kwa anthu. Timayanganila pasi anthu omwe ali mmavuto kumaganiza kuti anachita kubweretsa okha mavutowo. Mtima umenewu umatsekula makomo kwa satana kumiyoyo yanthu ndi ku utumiki.
Tsiku lina ndinakumana ndi azibusa atatu a mpingo wopambana wabwino. Gulu lawo logonjetsa linapangidwa ndi anthu awiri amphamvu othandizila ndi mbusa wamkulu. Mothandizidwa ndi omuthandizilawo Mbusayo anakwanisa kumanga tchalitchi imodzi yaikulu muzindawo. Zimaonneka kuti aliyese amakhamukila ku mpingo wawo. Mpingo watsopanowu unayamba kunyadila pa zovala ndipo amakhala ndi misonkhano ingapo ndi anthu ena kusefukila ndikukhala panja. Podzazidwa ndi chikondwerero pa zipambano zowo anayamba kuika maganizo awo pa zifukwa zomwe mpingo wina sumakula mu tawunimo.
Iwo ananena zonyoza mbusa wa mpingowo, Anthu amachoka mu mpingo pokhapokha ngati pali mtsogoleri oyipa. Izi ndi chifukwa cha utsogoleri oyipa kuti anthu achoka ku utumiki wake ndikuzajowina ife.
Nthawi imeneyo sindinaziwe ndikomwe kuti anthu amachoka ku mpingowo ndikukajowina wawowo. Ndimava koyamba kuti mpingowo unali ndi mtsogoleri oyipa. Kunali kovuta kudziwa chotonzedwa ndi mnyozo akamakamba za mpingowo ndi mtdogoleri oyipayo.
Eya, Sindimakaikira kuti anthu amachoka mu utumiki chifukwa cha utsogoleri oyipa. Koma muyenera kukhala osamala pa maweruzidwe ndi mfundo zanu.
Kwa zaka zambiri, atsogoleri atatu amenewa anatenga gawo lina la utumiki wawo. Gawo latsopano lililose limabweresa kusintha pa kugawa mofanana mphamvu. Mugawo latsopanoli othandizira awiri aja anamusiya mbusa wamkulu potumiza zipongwe ndi milandu kwa iye. Chilungamo ndichakuti kunyoza mbusa wina kuja kunawachitikira kwa iwo koma mu njira yoononga kwambiri.
Nditava za vutoli, choyamba chomwe chinachitika kwa ine ndichomwe amkanena za mpingo wa alongo awo ndi mbusa wawo, Anthu amakusiya pokhapokha ukakhala mtsogoleri oyipa.
Kod mbusa wakulu pano anali mtogoleri oyipa? Sikwenikweni. Pali zifukwa zambiri chifukwa chomwe anthu amakuchokerani. Koma onetsetsani kuti musatoze aliyese akakhala mmavuto.
Mudziko langa, pali mwambi omwe umati: Ukaona mzako akupsa ndevu usamuseke. Musafuse kuti analola bwanji ndevu zake kugwira moto. Inu katungeni madzi ndikuwasunga pambali panu kupangira zanu zikagwira moto.
Baibulo linati, …wokondwera ndi tsoka sadapulumuka chilango
(Miyambi 17:5)
5. Yehova amatha kulola anthu ena akusiyeni chifukwa tsogolo lanu silikhudzana nawo
Ana inu, ndi nthawi yotsiriza iyi; ndipo monga mudamva kuti wokana.Kristu akudza, ngakhale tsopano alipo okana Kristu ambiri; mwa ichi tizindikira kuti ndi nthawi yotsiriza iyi.
ANATULUKA MWA IFE, KOMATU SANALI A IFE ; pakuti akadakhala a ife akadakhalabe ndi ife koma kudatero kuti aonekekere kuti sali onse a ife
1 Yohane 2:18-19
Si aliyese oitanidwa kukhala mbali ya timu yanu. Ndi malingalilo achibadwidwe, timasankha anthu amene tikuona kuti akuenera kukhala nafe. Koma Mulungu anasankha kale anthu omwe ali mbali ya tsogolo lanu.
Kwa zaka ndakhala ndikukumana nazo zomalola anthu omwe ndimaona ngati azakhala nane mpaka kale kundichokera. Ndakhalaso ndi chosangalatsa chodabwitsa pokumana ndi alowammalo awo. Moona mtima, sindikanasankha anthu ambiri omwe ndilinawo lero. Koma Mulungu anawaitana kuzathandiza kumenya mu utumiki. Musamavutike anthu akachosedwa kwa inu. Nthawi zina zimakhala mkati mwa tsogolo lako kuti anachosedwa ndi kubweresa anthu olowammalo mwake.
6. Yehova amatha kulola anthu ena kuti akusiyeni kuti uvetsetse momwe Mulungu amavera ana ake akamusiya
Ndipo iye anati, Munthu wina anali ndi ana amuna awiri; ndipo wang’onoyo anati kwa atate wake, Atate, ndigailenitu zanga za pa chuma chanu. Ndipo iye anawagaira za moyo wake. Ndipo pakupita masiku owerengeka mwana wango’onoyo anasonkhanitsa zones napita ulendo wake ku dziko lakutari; ndipo komweko anamwaza chuma